Levitiko 2:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo munthu akabwera naco copereka ndico nsembe yaufa ya kwa Yehova, copereka cace cizikhala ca ufa wosalala; ndipo athirepo mafuta, ndi kuikapo libano.

2. Ndipo abwere nayo kwa ana a Aroni, ansembewo; natengeko ufa, ndi mafuta odzala manja, ndi libano wace wonse; ndipo wansembeyo aitenthe cikumbutso cace pa guwa la nsembe, ndiyo nsembe yamoto, ya pfungo lokoma la kwa Yehova.

3. Ndipo cotsalira ca nsembe yaufa cikhale ca Aroni ndi ana ace; ndico copatulikitsa ca nsembe zamoto za Yehova.

Levitiko 2