Levitiko 16:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo Aroni abwere nayo ng'ombe ya nsembe yaucimo, ndiyo yace yace, nacite codzitetezera iye yekha, ndi mbumba yace.

7. Ndipo atenge mbuzi ziwirizo naziimike pamaso pa Yehova pakhomo pa cihema cokomanako.

8. Ndipo Aroniayesemaere pa mbuzi ziwirizo; maere amodzi kwa Yehova, ndi amodzi kwa Azazeli.

9. Ndipo Aroni abwere nayo mbuzi imene adaigwera maere a Yehova, naiyese nsembe yaucimo.

10. Koma mbuzi imene adaigwera maere a Azazeli, aiike yamoyo pamaso pa Yehova, kuti acite nayo cotetezera, kuitumiza kucipululu ikhale ya Azazeli.

Levitiko 16