Levitiko 14:38-44 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

38. pamenepo wansembe azituruka ku khomo la nyumba, natseke nyumbayo masiku asanu ndi awiri;

39. ndipo wansembe abwerenso tsiku lacisanu ndi ciwiri, naonenso, ndipo taonani, ngati nthenda yakula m'makoma a nyumba;

40. pamenepo wansembe auze kuti agumule miyalayi pali nthenda, naitayire ku malo akuda kunja kwa mudzi;

41. napalitse nyumba m'kati monsemo, natayire ku malo akuda kunja kwa mudzi dothi adapalako;

42. natenge miyala yina, naikhazike m'male mwa miyala ija; natenge dothi tina, namatenso nyumbayo.

43. Ndipo ikabweranso nthenda, nibukanso m'nyumba atagumula miyala, ndipo atapala m'nyumba namatanso;

44. pamenepo wansembe alowe naonemo, ndipo taonani, ngati nthenda yakula m'nyumba, ndiyo khate lonyeka m'nyumba; ndiyo yodetsedwa.

Levitiko 14