Levitiko 11:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati nao,

2. Nenani ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Izi ndi zamoyo zimene muyenera kumadya mwa nyama zonse ziri pa dziko lapansi.

3. Nyama iri yonse yogawanika ciboda, nikhala yogawanikadi ciboda, ndi yobzikula, imeneyo muyenera kudya.

4. Koma izi zokha simuyenera kuzidya mwa zobzikulazo, kapena zogawanika ciboda; ngamila, angakhale abzikula, koma yosagawanika ciboda, muziiyesa yodetsedwa.

5. Ndi mbira, ingakhale ibzikula koma yosagawanika ciboda, muiyese yodetsedwa.

Levitiko 11