Hoseya 5:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo kudzikuza kwa Israyeli kudzamcitira umboni pamaso pace; cifukwa cace Israyeli ndi Efraimu adzakhumudwa m'mphulupulu mwao; Yudanso adzakhumudwa pamodzi nao.

6. Adzamuka ndi zoweta zao zazing'ono ndi zazikuru kufunafuna Yehova: koma sadzampeza; Iye wadzibweza kuwacokera.

7. Anacita mosakhulupirika pa Yehova, pakuti anabala ana acilendo; mwezi wokhala udzawatha tsopano, pamodzi ndi maiko ao.

8. Ombani mphalasa m'Gibeya, ndi lipenga m'Rama; pfuulani ku Betaveni; pambuyo pako, Benjamini.

9. Efraimu adzasanduka bwinja tsiku lakudzudzula; mwa mapfuko a Israyeli ndadziwitsa codzacitikadi.

Hoseya 5