Hagai 1:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Pamenepo mau a Yehova anadza mwa Hagai mneneri, ndi kuti,

4. Kodi imeneyi ndiyo nthawi yakuti inu nokha mukhala m'nyumba zanu zocingidwa m'katimo, ndi nyumba iyi ikhale yopasuka?

5. Cifukwa cace tsono, atero Yehova wa makamu: Mtima wanu usamalire njira zanu.

6. Mwabzala zambiri, koma mututa pang'ono; mukudya, koma osakhuta; mukumwa, koma osakoledwa; mudzibveka, koma palibe wofundidwa; ndi iye wolembedwa nchito yakulipidwa alandirira kulipirako m'thumba lobooka.

Hagai 1