13. Ndipo Hagai mthenga wa Yehova m'uthenga wa Yehova ananena ndi anthu, ndi kuti, Ine ndiri nanu, ati Yehova.
14. Ndipo Yehova anautsa mzimu wa Zerubabele mwana wa Sealitiyeli, ciwanga ca Yuda, ndi mzimu wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndi mzimu wa otsala onse a anthu, ndipo anadza nagwira nchito m'nyumba ya Yehova wa makamu, Mulungu wao,
15. tsiku la makumi awiri ndi anai la mwezi, mwezi wacisanu ndi cimodzi, caka caciwiri ca mfumu Dariyo.