Genesis 9:4-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Koma nyama, m'mene muli moyo wace, ndiwo mwazi wace, musadye.

5. Zoonatu mwazi wanu wa miyoyo yanu ndidzafuna; pa dzanja la zinyama zonse ndidzaufuna: ndi pa dzanja la munthu, pa dzanja la mbale wace wa munthu ndidzaufuna moyo wa munthu.

6. Amene akhetsa mwazi wa munthu, ndi munthunso mwazi wace udzakhetsedwa: cifukwa m'cifanizo ca Mulungu Iye anampanga munthu.

7. Ndi inu, mubalane, mucuruke; muswane pa dziko lapansi, nimucuruke m'menemo.

8. Ndipo Mulungu ananena kwa Nowa ndi kwa ana ace pamodzi naye, kuti,

9. Ndipo Ine, taonani, Ine ndikhazikitsa pangano langa pamodzi ndi inu, ndi mbeu zanu pambuyo panu;

10. ndi zamoyo zonse ziti pamodzi ndi inu, zouluka, ng'ombe, ndi zinyama zonse za dziko lapansi, pamodzi ndi inu; zonse zoturuka m'cingalawa, zinyama zonse za dziko lapansi,

Genesis 9