Genesis 9:24-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Nowa ndipo anauka kwa kuledzera kwace, nadziwa cimene anamcitira iye mwana wace wamng'ono.

25. Ndipo anati,Wotembereredwa ndi Kanani:Adzakhala kwa abale ace kapolo wa akapolo:

26. Ndipo anati:Ayamikike Yehova, Mulungu wa Semu;Kanani akhale kapolo wace.

27. Mulungu akuze Yafeti,Akhale iye m'mahema a Semu; Kanani akhale kapolo wace.

28. Ndipo Nowa anakhala ndi moyo cigumula citapita, zaka mazana atatu kudza makumi asanu.

29. Ndipo masiku onse a Nowa anali mazana asanu ndi anai kudza makumi asanu: ndipo anamwalira.

Genesis 9