Genesis 9:2-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Kuopsya kwanu, ndi kucititsa mantha kwanu kudzakhala pa zinyama zonse za dziko lapansi, ndi pa zouluka zonse za m'mlengalenga; ndi pa zonse zokwawa pansi, ndi pa nsomba zonse za m'nyanja, zapatsidwa m'dzanja lanu.

3. Zoyenda zonse zamoyo zidzakhala zakudya zanu; monga therere laliwisi ndakupatsani inu zonsezo.

4. Koma nyama, m'mene muli moyo wace, ndiwo mwazi wace, musadye.

5. Zoonatu mwazi wanu wa miyoyo yanu ndidzafuna; pa dzanja la zinyama zonse ndidzaufuna: ndi pa dzanja la munthu, pa dzanja la mbale wace wa munthu ndidzaufuna moyo wa munthu.

6. Amene akhetsa mwazi wa munthu, ndi munthunso mwazi wace udzakhetsedwa: cifukwa m'cifanizo ca Mulungu Iye anampanga munthu.

7. Ndi inu, mubalane, mucuruke; muswane pa dziko lapansi, nimucuruke m'menemo.

8. Ndipo Mulungu ananena kwa Nowa ndi kwa ana ace pamodzi naye, kuti,

Genesis 9