Genesis 9:2-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Kuopsya kwanu, ndi kucititsa mantha kwanu kudzakhala pa zinyama zonse za dziko lapansi, ndi pa zouluka zonse za m'mlengalenga; ndi pa zonse zokwawa pansi, ndi pa nsomba zonse za m'nyanja, zapatsidwa m'dzanja lanu.

3. Zoyenda zonse zamoyo zidzakhala zakudya zanu; monga therere laliwisi ndakupatsani inu zonsezo.

4. Koma nyama, m'mene muli moyo wace, ndiwo mwazi wace, musadye.

Genesis 9