Genesis 8:19-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. zinyama zonse, zokwawa zonse, zouluka zonse, ndi zonse zokwawa pa dziko lapansi, monga mwa mitundu yao, zinaturuka m'cingalawamo.

20. Ndipo Nowa anamanga guwa la nsembe la Yehova; natengapo nyama zodyedwa zonse ndi mbalame zodyedwa zonse napereka nsembe zopsereza paguwapo.

21. Ndipo Yehova anamva conunkhira cakukondweretsa; nati Yehova m'mtima mwace, Sindidzatembereranso konse nthaka cifukwa ca munthu; pakuti ndingaliro ya mtima wa munthu iri yoipa kuyambira pa unyamata wace; sindidzaphanso konse zinthu zonse zamoyo, monga momwe ndacitiramo.

22. Pakukhalabe masiku a dziko lapansi, nthawi yakubzala ndi yakukunkha, cisanu ndi mafundi, malimwe ndi msakasa, usana ndi usiku sizidzalekai.

Genesis 8