Genesis 42:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo Yosefe anazindikira abale ace, koma iwo sanamzindikira iye.

9. Ndipo Yosefe anakumbukira maloto amene analoto za iwo, ndipo anati kwa iwo, Ozonda inu; mwadzera kudzaona usiwa wa dziko.

10. Ndipo iwo anati kwa iye, Iai, mbuyanga, koma akapolo anu adzera kudzagula cakudya.

11. Tonse tiri ana amuna a munthu mmodzi; tiri oona, akapolo anu, sitiri ozonda.

12. Ndipo iye anati kwa iwo, Iai, koma mwadzera kuti muone usiwa wa dziko.

Genesis 42