Genesis 42:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anaona Yakobo kuti m'Aigupto munali tirigu, nati Yakobo kwa ana ace amuna, Cifukwa canji mulinkuyang'anana?

2. Ndipo iye anati, Taonani, ndamva kuti m'Aigupto muli tirigu, mutsikireko mutigulire kumeneko; kuti tikhale ndi moyo, tisafe.

3. Ndipo abale ace a Yosefe khumi anatsikira kukagula tirigu m'Aigupto.

4. Koma Yakobo sanamtuma Benjamini mphwace wa Yosefe, pamodzi ndi abale ace, cifukwa anati, Coipa cingamgwere iye.

Genesis 42