Genesis 31:51-53 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

51. Ndipo Labani anati kwa Yakobo. Taona muluwu, taona coimiritsaci, ndaciimiritsa pakati pathu.

52. Muluwu ndiwo mboni, coimiritsaci ndico mboni, kuti ine sindidzapitirira pa muluwu kunka kwa iwe, ndipo iwe sudzapitirira pa muluwu ndi pa coimiritsaci kudza kwa ine kuti ticitirane zoipa,

53. Mulungu wa Abrahamu ndi Mulungu wa Nahori, Mulungu wa atate wao aweruze pa ife. Ndipo Yakobo analumbirira pa Kuopsa kwa atate wace Isake.

Genesis 31