Genesis 31:46-49 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

46. Ndipo Yakobo anati kwa abale ace, Sonkhanitsani miyala; ndipo anasonkhanitsa miyala nakundika mulu: ndipo anadya pamulupo.

47. Ndipo Labani anacha pamenepo Yegara-sahaduta; koma Yakobo anacha Galeeda.

48. Ndipo Labani anati, Muluwu ndiwo mboni pakati pa ine ndi iwe lero. Cifukwa cace anacha dzina lace, Galeeda;

49. ndi Mizipa, cifukwa kuti anati, Yehova ayang'anire pakati pa ine ndi iwe, pamene tisiyana wina ndi mnzace.

Genesis 31