Genesis 31:16-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Cifukwa kuti cuma conse Mulungu anacicotsa kwa atate wathu ndi cathu ndi ca ana athu; tsono, zonse wakunenera iwe Mulungu, ucite.

17. Ndipo anauka Yakobo nakweza ana ace ndi akazi ace pa ngamila;

18. ndipo ananka nazo zoweta zace zonse, ndi cuma cace conse anacisonkhanitsa, zoweta zace anaziona m'Padan-aramu, kuti anke kwa Isake atate wace ku dziko la Kanani.

19. Ndipo Labani ananka kukasenga nkhosa zace: ndipo Rakele anaba aterafi a atate wace.

20. Ndipo Yakobo anathawa kwa Labani Msuriyamobisika, m'mene sanamuuzeiye kuti analinkuthawa.

21. Ndipo anathawa iye ndi zonse anali nazo: ndipo anauka naoloka panyanja naloza nkhope yace iyaog'anire ku phiri la Gileadi.

22. Tsiku lacitatu anamuuza Labani kuti Yakobo wathawa.

Genesis 31