Genesis 3:12-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo anati mwamunayo, Mkazi amene munandipatsa ine kuti akhale ndi ine, ameneyo anandipatsa ine za mtengo, ndipo ndinadya.

13. Ndipo Yehova Mulungu anati kwa mkaziyo, Ciani cimene wacitaci? Ndipo anati mkaziyo, Njoka inandinyenga ine, ndipo ndinadya.

14. Ndipo anati Yehova Mulungu kwa njokayo, Cifukwa kuti wacita ici, wotembereredwa ndiwe wopambana ndi zinyama zonse ndi zamoyo zonse za m'thengo: uziyenda ndi pamimba pako, uzidya pfumbi masiku onse a moyo wako:

15. ndipo ndidzaika udani pakati pa iwe ndi mkaziyo, ndi pakati pa mbeu yako ndi mbeu yace; ndipo idzalalira mutu wako, ndipo iwe udzalalira citende cace.

Genesis 3