Genesis 27:37-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. Ndipo anayankha Isake nati kwa Esau, paona, ndamuyesa iye mkuru wako, ndi abale ace onse ndampatsa iye akhale akapolo ace; ndakhazikitsa iye ndi tirigu ndi vinyo; nanga pamenepo mwana wanga, ndidzakucitira iwe ciani?

38. Ndipo Esau anati kwa atate wace, Kodi muli nao mdalitso umodzi wokha, atate wanga? Mundidalitse ine, inenso, atate wanga, Ndipo Esau anakweza mau ace nalira.

39. Ndipo Isake atate wace anayankha nati kwa iye,Taona, pokhala pako mpa zonenepa za dziko lapansi,Mpa mame a kumwamba akudzera komwe;

40. Udzakhala ndi moyo ndi lupanga lako, nudzakhala kapolo wamphwako;Ndipo padzakhalapamene udzapulumuka,Udzacotsa gori lace pakhosi pako.

41. Ndipo Esau anamuda Yakobo cifukwa ca mdalitso umene atate wace anamdalitsa nao: ndipo Esau anati m'mtima mwace, Masiku a maliro a atate wanga ayandikira; pamenepo ndipo ndidzamupha mphwanga Yakobo.

Genesis 27