Genesis 27:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo panali atakalamba Isake, ndi maso ace anali a khungu losaona nalo, anamuitana Esau mwana wace wamwamuna wamkuru, nati kwa iye, Mwana wanga; ndipo anati kwa iye, Ndine pano.

2. Ndipo anati, Taonatu, ndakalamba, sindidziwa tsiku la kufa kwanga:

3. tsopano tengatu zida zako ndi phodo lako ndi uta wako, numuke kuthengo kundisakira ine nyama;

4. nundikonzere ine cakudya cokolera conga comwe ndicikonda ine, nudze naco kwa ine kuti ndidzadye; kuti moyo wanga ukadalitse iwe ndisanafe.

Genesis 27