21. Ndipo anakumbanso citsime cina, ndipo anakangana naconso; nacha dzina lace Sitina.
22. Ndipo anacoka kumeneko nakumba citsime cina; koma sanakangana naco cimeneco; ndipo anacha dzina lace Rehoboti; ndipo anati, Cifukwa kuti tsopano Yehova anatipatsa ife malo, ndipo tidzabalana m'dziko muno.
23. Ndipo anacoka kumeneko nakwera kunka ku Beereseba,