4. Ine ndine mlendo wakukhala ndi inu: mundipatse ndikhale ndi manda pamodzi ndi inu, kuti ndiike wakufa wanga ndisamthirenso maso.
5. Ndipo ana a Heti anayankha Abrahamu nati kwa iye,
6. Mutimvere ife mfumu, ndinu karonga wamkuru pakati pa ife; muike wakufa wanu m'manda mwathu mosankhika: palibe munthu yense wa ife adzakaniza manda ace, kuti muike wakufa wanu.
7. Ndipo anauka Abrahamu naweramira anthu a m'dzikomo, ana a Heti.