Genesis 23:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ine ndine mlendo wakukhala ndi inu: mundipatse ndikhale ndi manda pamodzi ndi inu, kuti ndiike wakufa wanga ndisamthirenso maso.

5. Ndipo ana a Heti anayankha Abrahamu nati kwa iye,

6. Mutimvere ife mfumu, ndinu karonga wamkuru pakati pa ife; muike wakufa wanu m'manda mwathu mosankhika: palibe munthu yense wa ife adzakaniza manda ace, kuti muike wakufa wanu.

7. Ndipo anauka Abrahamu naweramira anthu a m'dzikomo, ana a Heti.

Genesis 23