2. Ndipo ndidzapangana pangano langa ndi Ine ndi iwe, ndipo ndidzacurukitsa iwe kwambiri.
3. Ndipo Abramu anagwa nkhope pansi, ndipo Yehova ananena naye kuti,
4. Koma Ine, taona, pangano langa liri ndi iwe, ndipo udzakhala iwe atate wa khamu la mitundu.
5. Sudzachedwanso dzina lako Abramu, koma dzina lako lidzakhala Abrahamu; cifukwa kuti ndakuyesa iwe atate wa khamu la mitundu.