Genesis 1:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. PACIYAMBI Mulungu adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.

2. Dziko lapansi ndipo linali lopanda kanthu; ndipo mdima unali pamwamba pa nyanja; ndipo mzimu wa Mulungu unaliokufungatira pamwamba pa madzi.

3. Ndipo anati Mulungu, Kuyere; ndipo kunayera.

4. Ndipo anaona Mulungu kuti kuyerako kunali kwabino: ndipo Mulungu analekanitsa kuyera ndi mdima.

5. Ndipo Mulungu anacha kuyerako Usana, ndi mdimawo anaucha Usiku. Ndipo panali madzulo ndipo panali m'mawa, tsiku loyamba.

Genesis 1