Ezekieli 5:15-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Momwemo cidzakhala cotonza ndi mnyozo, cilangizo ndi codabwiza kwa amitundu akukuzinga, pamene ndikucitira maweruzo mu mkwiyo ndi ukali ndi madzudzulo aukali; Ine Yehovandanena.

16. Pakuwatumizira Ine mibvi yoipa ya njala yakuononga, imene ndidzatumiza kukuonongani, pamenepo ndidzakukuzirani njala, ndi kukutyolerani mcirikizo, ndiwo cakudya.

17. Inde ndidzakutumizirani njala ndi zirombo, ndipo zidzakusowetsa ana ako; ndi mliri ndi mwazi zidzakugwera; ndidzakufikitsiranso lupanga; Ine Yehova ndacinena.

Ezekieli 5