24. Nakonze nsembe yaufa, ku ng'ombe kukhale efa; ndi ku nkhosa yamphongo kukhale efa; ndi kuefa kukhale hini wa mafuta.
25. Mwezi wacisanu ndi ciwiri, tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi, pamadyerero, acite momwemo masiku asanu ndi awiri, monga mwa nsembe yaucimo, monga mwa nsembe yopsereza, ndi monga mwa nsembe yaufa, ndi monga mwa mafuta.