Ezekieli 45:20-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Tsiku lacisanu ndi ciwiri la mweziwo ucitire momwemo ali yense wolakwa ndi wopusa; motero mucitire kacisiyo comtetezera.

21. Mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi cinai la mwezi, muzicita Paskha, madyerero a masiku asanu ndi awiri; audye mkate wopanda cotupitsa.

22. Ndipo tsiku lomwelo kalonga adzikonzere yekha ndi anthu onse a m'dziko ng'ombe, ikhale ya nsembe yaucimo.

23. Ndipo masiku asanu ndi awiri a madyerero akonzere Yehova nsembe yopsereza, ng'ombe zisanu ndi ziwiri, ndi nkhosa zamphongo zisanu ndi ziwiri zopanda cirema, tsiku ndi tsiku, masiku asanu ndi awiriwa; ndi tonde tsiku ndi tsiku, akhale wa nsembe yaucimo.

24. Nakonze nsembe yaufa, ku ng'ombe kukhale efa; ndi ku nkhosa yamphongo kukhale efa; ndi kuefa kukhale hini wa mafuta.

Ezekieli 45