3. Ndipo maonekedwe a masomphenya ndinawaona anali monga masomphenya aja ndinawaona pakudza ine kupasula mudzi; ndi masomphenyawa anali ngati masomphenya aja ndinawaona ku mtsinje wa Kebara; ndipo ndinagwa nkhope pansi.
4. Ndipo ulemerero wa Yehova unalowa m'kacisi kudzera njira ya cipata coloza kum'mawa.
5. Ndipo mzimu unandinyamula numuka nane ku bwalo la m'kati; ndipo taonani, ulemerero wa Mulungu unadzaza kacisi.
6. Ndipo ndinamva wina alikulankhula nane ali m'kacisi, naima nane munthu.