Ezekieli 42:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Pakuti zinasanjikizana pawiri, ndipo zinalibe nsanamira ngati nsanamira za kumabwalo; cifukwa cace zam'mwambazo zinacepa koposa zakunsi ndi zapakati kuyambira pansi.

7. Ndipo linga linali kunialo, loli'ngana ndi nyumba yazipinda, kuloza ku bwalo lakunja, popenyana ndi nyumba yazipinda, m'litali mwace munali mikono makumi asanu.

8. Pakuti kupingasa kwace kwa nyumba yazipinda inali m'bwalo lakunja, kunali mikono makumi asanu; ndipo taonani, kuloza ku khomo la Kacisi inali mikono zana limodzi.

9. Ndipo pansi pa zipinda izi panali polowera mbali ya kum'mawa, poloweramo kucoka ku bwalo lakunja.

10. M'kucindikira kwa linga la bwalo, kuloza kumwera, cakuno ca mpatawo, cakuno ca nyumba, panali nyumba yazipinda.

Ezekieli 42