Ezekieli 41:9-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Kucindikira kwa khoma la kuzipinda za m'mphepete kunja kwace kunali mikono isanu; ndipo mpata wace unali malo olowera m'zipinda za m'mphepete za kacisi.

10. Ndi pakati pa zipinda panali kupingasa kwa mikono makumi awiri, pozungulira pace ponse pa nyumba.

11. Ndi makomo a zipinda za m'mphepete analoza kumpatawo, khomo lina kumpoto, ndi lina kumwela; ndi malo a pa mpatawo anayesa mikono isanu kupingasa kwace pozungulira pace.

12. Ndipo nyumba inali kutsogolo kwa mpata wa mbali ya kumadzulo inali ya mikono makumi asanu ndi awiri kupingasa kwace; ndi khoma la nyumbayo pozungulira pace linali la mikono isanu kucindikira kwace; ndi m'litali mwace mikono makumi asanu ndi anai.

Ezekieli 41