Ezekieli 4:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo cakudya cako uzicidya ciyesedwe masekeli makumi awiri tsiku limodzi; uzidyako tsiku ndi tsiku pa nthawi yace.

11. Uzimwanso madzi monga mwa muyeso, limodzi la magawo asanu ndi limodzi la hini; uzimwako tsiku ndi tsiku pa nthawi yace.

12. Ndipo uzicidya ngati timikate ta barele, ndi kutioca pamaso pao ndi zonyansa za munthu.

13. Ndipo Yehova anati, Motero ana a Israyeli adz adya ca kudya cao codetsedwa, mwa amitundu kumene ndidzawaingitsirako.

14. Pamenepo ndinati, Ha, Ambuye Yehova! taonani, moyo wanga sunadetsedwa, pakuti ciyambire ubwana wanga mpaka tsopano sindinadye cinthu cakufa cokha, kapena cogwidwa ndi cirombo; simunalowanso m'kamwa mwanga nyama yonyansa.

Ezekieli 4