Ezekieli 37:17-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. nuiphatikize wina ndi unzace ikhale mtengo umodzi m'dzanja lako.

18. Ndipo ana a anthu amtundu wako akanena ndi iwe, ndi kuti, Sutifotokozera nanga zitani izi?

19. unene nao, Atero Ambuye Yehova, Taonani, ndidzatenga mtengo wa Yosefe uli m'dzanja la Efraimu, ndi wa mafuko a Israyeli anzace, ndi kuwaika pamodzi ndi mtengo wa Yuda, ndi kuiyesa mtengo umodzi; ndipo idzakhala umodzi m'dzanja langa.

20. Ndipo mitengo imene ulembapo idzakhala m'dzanja mwako pamaso pao.

21. Nunene nao, Atero Ambuye Yehova, Taonani, ndidzatenga ana a Israyeli pakati pa amitundu kumene adamkako, ndi kuwasokolotsa ku mbali zonse, ndi kulowa nao m'dziko mwao;

Ezekieli 37