Ezekieli 35:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndidzapasula midzi yako, nudzakhala lacipululu; ndipo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

5. Popeza uli nao udani wosatha, waperekanso ana a Israyeli ku mphamvu ya lupanga m'nthawi ya tsoka lao, mu nthawi ya mphulupulu yotsiriza;

6. cifukwa cace, Pali Ine, ati Ambuye Yehova, ndikukonzeratu uphedwe, ndi mwazi udzakulondola; popeza sunadana nao mwazi, mwazi udzakulondola.

7. Ndipo ndidzaika phiri la Seiri lodabwitsa ndi lacipululu, ndi kuononga pomwepo wopitapo ndi wobwerapo.

Ezekieli 35