1. Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,
2. Wobadwa ndi munthu iwe, Nena ndi ana a anthu a mtundu wako, uziti nao, Ndikafikitsira dziko liri lonse lupanga, nakatenga eni dziko munthu wa pakati pao, nakamuika awadikirire,
3. nakaona iye lupanga lirikudzera dziko, nakaomba lipenga ndi kucenjeza anthu;
4. ndipo wina, kumva adamva mau a lipenga, koma osalabadira, likadza lupanga, nilimcotsa, wadziphetsa ndi mtima wace.