Ezekieli 29:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Caka cakhumi, mwezi wakhumi, tsiku lakhumi ndi ciwiri la mweziwo, anandidzera mau a Yehova, akuti,

2. Wobadwa ndi munthu iwe, lozetsa: nkhope yako itsutsane naye Farao mfumu ya Aigupto, nunenere motsutsana ndi iye, ndi Aigupto lonse;

3. nena, uziti, Atero Ambuye Yehova, Taona nditsutsana nawe, Farao mfumu ya Aigupto, ng'ona yaikuru yakugona m'kati mwa mitsinje yace, imene ikuti, Mtsinje wanga ndi wangatu, ndadzipangira ndekha uwu.

4. Koma ndidzaika mbedza m'kamwa mwako, ndi kumamatiritsa nsomba za m'mitsinje mwako ku mamba ako; ndipo ndidzakukweza kukuturutsa m'kati mwa mitsinje yako, pamodzi ndi nsomba zonse za m'mitsinje mwako zomamatira pa mamba ako.

Ezekieli 29