1. Koma podziwa Moredekai zonse zidacitikazi, Moredekai anang'amba zobvala zace, nabvala ciguduli ndi mapulusa, naturuka pakati pa mudzi, napfuula, nalira kulira kwakukuru ndi kowawa,
2. nafika popenyana ndi cipata ca mfumu; popeza sanathe munthu kulowa ku cipata ca mfumu wobvala ciguduli.