Eksodo 8:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo acule adzakwera pa iwe, ndi pa anthu ako, ndi pa anyamata ako onse.

5. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Nena ndi Aroni, Tambasula dzanja lako ndi ndodo yako, panyanja, pangalande, ndi pamatamanda, nukweretse acule pa dziko la Aigupto.

6. Ndipo Aroni anatambasula dzanja lace pa madzi a m'Aigupto; ndipo anakwera acule, nakuta dziko la Aigupto.

7. Ndipo alembi anacita momwemo ndi matsenga ao, nakweretsa acule pa dziko la Aigupto.

Eksodo 8