Eksodo 8:28-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Ndipo Farao anati, Ndidzakulolani mumuke, kuti mukamphere nsembe Yehova. Mulungu wanu m'cipululu; komatu musamuke kutaritu: mundipembere.

29. Ndipo Mose anati, Onani, ndirikuturuka ine kwanu, ndidzapemba Yehova kuti mizaza icoke mawa kwa Farao, ndi kwa anyamata ace, ndi kwa anthu ace; komatu, Farao asanyengenso ndi kukana kulola anthuwa amuke kukamphera nsembe Yehova.

30. Ndipo Mose anaturuka kwa Farao, napemba Yehova.

31. Ndipo Yehova anacita monga mwa mau a Mose; nacotsera Farao ndi anyamata ace ndi anthu ace mizazayo, sunatsala ndi umodzi wonse.

32. Koma Farao anaumitsa mtima wace nthawi yomweyonso, ndipo sanalola anthu amuke.

Eksodo 8