13. Nubveke Aroni cobvala zopatulikazo; ndi kumdzoza, ndi kumpatwa andicitire Ine nchito ya nsembe.
14. Ndipo ubwere nao ana ace amuna ndi kuwabveka maraya am'kati;
15. nuwadzoze, monga unadzoza atate wao, kuti andicitire nchito ya nsembe; ndi kudzozedwa kwao kuwakhalire unsembe wosatha mwa mibadwo yao.
16. Anatero Mose; monga mwa zonse Yehova adamuuza, momwemo anacita.