Eksodo 38:3-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Anapanganso zipangizo zonse za guwalo, zotayira, ndi zoolera, ndi mbale zowazira, ndi mitungo, ndi zoparira moto; zipangizo zace zonse anazipanga zamkuwa.

4. Ndipo anapangira guwa La nsembelo made, malukidwe ace nja mkuwa, pansi pa matso ace wakulekeza pakati pace.

5. Ndipo anayengera mathungo anai a made amkuwawo mphete zinai, zikhale zopisamo mphiko.

6. Napanga mphiko za mtengo wasitimu, nazikuta ndi mkuwa.

7. Ndipo anapisa mphikozo m'zimphetemo pa mbali za guwa la nsembe, kulinyamulira nazo; analipanga ndi matabwa, lagweregwere.

8. Ndipo anapanga mkhate wamkuwa, ndi tsinde lace lamkuwa, wa akalirole a akazi otumikira, akutumikira pa khomo la cihema cokomanako.

9. Ndipo anapanga bwalo; pa mbali ya kumwela, kumwela, nsaru zocingira za pabwalo zinali za bafuta wa thonje losansitsa, mikono zana limodzi;

10. nsici zace makumi awiri, ndi makamwa ao makumi awiri, amkuwa; zokowera za nsici ndi mitanda yace zasiliva.

11. Ndi pa mbali ya kumpoto mikono zana limodzi, nsici zace makumi awiri, nw makamwa ace makumi awiri, amkuwa; zokowera za nsici ndi mitanda yace yasiliva.

12. Ndi pa mbali ya kumadzulo panali nsaru zocingira za mikono makumi asanu, nsid zace khumi, ndi makamwa ace khumi; zokowera za nsici ndi mitanda yace yasiliva.

Eksodo 38