Eksodo 35:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. ndi mafuta akuunikira, ndi zonunkhira za mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma;

9. ndi miyala yasohamu, ndi miyala yoika ya efodi, ndi ya capacifuwa.

10. Ndipo abwere yense wa mtima waluso mwa inu, napange zonse zimene Yehova anauza;

11. kacisi, hema wace, ndi cophimba cace, zokowera zace, ndi matabwa ace, mitanda yace, mizati, nsanamira, ndi nsici zace, ndi makamwa ao;

12. likasa, ndi mphiko zace, cotetezerapo, ndi nsaru yocinga yotseka;

Eksodo 35