Eksodo 35:26-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Ndi akazi onse ofulumidwa mtima ndi luso anapota ubweyawo wa mbuzi.

27. Ndi akuru anabwera nayo miyala yasohamu, ndi miyala yoti aiike kuefodi, ndi kucapacifuwa;

28. ndi zonunkhira, ndi mafuta akuunikira, ndi mafuta odzoza, ndi cofukiza za pfungo lokoma.

29. Amuna ndi akazi onse a ana a Israyeli amene mitima yao inawafunitsa eni kubwera nazo za ku nchito yonse imene Yehova anauza Ipangike ndi dzanja la Mose, anabwera naco copereka cofuna mwini, kucipereka kwa Yehova.

Eksodo 35