Eksodo 33:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ananenanso, Sungathe kuona nkhope yanga; pakuti palibe munthu adzandiona Ine ndi kukhala ndi moyo.

21. Ndipo Yehova anati, Taona pali Inepo pali malo, ndipo uime pathanthwe;

22. ndipo kudzakhala, pakupitira olemerero wanga, ndidzakuika mu mpata wa thanthwe, ndi kukuphimba ndi dzanja langa, mpaka nditapitira;

23. ndipo pamene ndicotsa dzanja langa udzaona m'mbuyo mwanga; koma nkhope yanga siidzaoneka.

Eksodo 33