14. Ndipo Yehova analeka coipa adanenaci, kuwacitira anthu ace.
15. Ndipo Mose anatembenuka, natsika m'phirimo, magome awiri a mboni ali m'dzanja lace; magome olembedwa kwina ndi kwina; analembedwa mbali yina ndi inzace yomwe.
16. Ndipo magomewo ndiwo nchito ya Mulungu, kulembaku ndiko kulemba kwa Mulungu, kozokoteka pa magomewo.