Eksodo 29:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Pamenepo utenge mafuta odzoza nao nuwatsanulire pamutu pace, ndi kumdzoza.

8. Ndipo ubwere nao ana ace amuna ndi kuwabveka maraya am'kati.

9. Uwamangirenso Aroni ndi ana ace amuna mipango m'cuuno mwao, nuwamangire akapa pamutu pao; ndipo akhale ansembe mwa lemba losatha; nudzaze dzanja la Aroni ndi dzanja la ana ace amuna,

10. Ndipo ubwere nayo ng'ombe yamphongo patsogolo pa cihema cokomanako; ndipo Aroni ndi ana ace amuna aike manja ao pamutu pa ng'ombe yamphongoyo.

Eksodo 29