Eksodo 29:43-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

43. Ndipo pamenepo ndidzakomana ndi ana a Israyeli; ndipo cihema cidzapatulidwa ndi ulemerero wanga.

44. Ndipo ndidzapatula cihema cokomanako, ndi guwa la nsembe; ndidzapatulanso Aroni ndi ana ace amuna omwe, andicitire nchito ya nsembe.

45. Ndipo ndidzakhala pakati pa ana a Israyeli, ndi kukhala Mulungu wao.

46. Ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wao, amene ndinawaturutsa m'dziko la Aigupto, kuti ndikhale pakati pao. Ine ndine Yehova Mulungu wao.

Eksodo 29