Eksodo 23:21-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Musamalire iye, ndi kumvera mau ace; musamwawitsa mtima, pakuti sadzakhululukira zoo lakwa zanu; popeza dzina langa liri m'mtima mwace.

22. Pakuti ukamveratu mau ace, ndi kucita zonse ndizilankhula, ndidzakhala mdani wa adani ako, ndipo ndidzasautsa akusautsa iwe.

23. Pakuti mthenga wanga adzakutsogolera, nadzakufikitsa kwa Aamori, ndi Ahiti, ndi Aperizi, ndi Akanani, Ahivi, ndi Ayebusi; ndipo ndidzawaononga.

Eksodo 23