21. Ndipo anthu anaima patali, koma Mose anayandikiza ku mdima waukuru kuli Mulungu.
22. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Uzitero ndi ana a Israyeli, kuti, Mwapenya nokha kuti ndalankhula nanu, kucokerakumwamba.
23. Musapange milungu yasiliva ikhale pamodzi ndi Ine; musadzipangire milungu yagolidi.
24. Undiumbire guwa la nsembe ladothi, nundiphere pomweponsembe zako zopsereza, ndi nsembe zako zamtendere, nkhosa zako ndi ng'ombe zako; pali ponse ndikumbukiritsa anthu dzina langa ndidzakudzera ndi kukudalitsa.
25. Ndipo ukandimangira guwa la nsembe lamiyala, usalimanga ndi miyala yosema; ukakwezapo cosemera cako, waliipsa.
26. Kapena usakwere ndi makwerero ku guwa langa la nsembe, kuti angaoneke marisece ako pamenepo.