Eksodo 10:25-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Koma Mose anati, Mutipatsenso m'dzanja mwathu nsembe zophera ndi nsembe zopsereza, kuti timkonzere Yehova Mulungu wathu.

26. Zoweta zathu zomwe tidzapita nazo; cosatsala ciboda cimodzi; pakuti mwa izo tiyenera kutenga zakutumikira nazo Yehova Mulungu wathu; ndipo tisanafikeko, sitidziwa umo tidzamtumikira Yehova.

27. Koma Yehova analimbitsa mtima wace wa Farao, ndipo anakana kuwaleka amuke.

28. Ndipo Farao ananena naye, Coka pano, uzicenjera usaonenso nkhope yanga; pakuti tsiku limene uonanso nkhope yanga udzafa.

29. Ndipo Mose anati, Mwanena bwino; sindidzaonanso nkhope yanu.

Eksodo 10