12. Koma monga momwe anawasautsiramo, momwemo anacuruka, momwemonso anafalikira. Ndipo anabvutika cifukwa ca ana a Israyeli.
13. Ndipo Aaigupto anawagwiritsa ana a Israyeli nchito yosautsa;
14. nawawitsa moyo wao ndi nchito yolimba, ya dothi ndi ya njerwa, ndi nchito zonse za pabwalo, nchito zao zonse zimene anawagwiritsa nzosautsa.
15. Ndipo mfumu ya Aigupto inanena ndi anamwino a Ahebri, dzina lace la wina ndiye Sifra, dzina la mnzace ndiye Puwa;